Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 132:13 - Buku Lopatulika

pakuti Yehova anasankha Ziyoni; analikhumba likhale pokhala pake; ndi kuti,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

pakuti Yehova anasankha Ziyoni; analikhumba likhale pokhala pake; ndi kuti,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta wasankhula Ziyoni, akufuna kuti akhale malo ake okhalamo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

Onani mutuwo



Masalimo 132:13
11 Mawu Ofanana  

komatu sindidzachotsa ufumu wonsewo; fuko limodzi ndidzapatsa mwana wako, chifukwa cha Davide mtumiki wanga, ndi chifukwa cha Yerusalemu amene ndinamsankha.


Pakuti ndasankha ndi kuipatula nyumba iyi, kuti dzina langa likhaleko chikhalire; inde maso anga ndi mtima wanga zidzakhala komweko kosalekeza.


Aliyense mwa inu a anthu ake onse, Mulungu wake akhale naye, akwere kunka ku Yerusalemu, ndiwo mu Yuda, nakaimange nyumba ya Yehova Mulungu wa Israele; Iye ndiye Mulungu wokhala mu Yerusalemu.


Muchitiranji nsanje mapiri inu a mitumitu, ndi phirilo Mulungu analikhumba, akhaleko? Inde, Yehova adzakhalabe komweko kosatha.


Yehova akonda zipata za Ziyoni koposa zokhalamo zonse za Yakobo.


Pakuti Iye wofuna chamwazi awakumbukira; saiwala kulira kwa ozunzika.


Ndipo adzayankhanji amithenga a amitundu? Kuti Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo m'menemo anthu ake ovutidwa adzaona pobisalira.


Komatu mwayandikira kuphiri la Ziyoni, ndi mzinda wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wa Kumwamba, ndi kwa unyinji wochuluka wa angelo,