Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 132:1 - Buku Lopatulika

Yehova, kumbukirani Davide kuzunzika kwake konse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova, kumbukirani Davide kuzunzika kwake konse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, mukumbukire Davide ndi mavuto onse amene adaŵapirira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.

Onani mutuwo



Masalimo 132:1
20 Mawu Ofanana  

Ndipo Mulungu anakumbukira Nowa ndi zamoyo zonse, ndi nyama zonse zimene zinali pamodzi naye m'chingalawamo; ndipo Mulungu anapititsa mphepo padziko lapansi, naphwa madzi;


Ndinafuulira kwa Yehova mu msauko wanga, ndipo anandivomereza.


Ndikweza maso anga kumapiri: Thandizo langa lidzera kuti?


Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni kunyumba ya Yehova.


Ndikweza maso anga kwa Inu, kwa Inu wakukhala kumwamba.


Akadapanda kukhala nafe Yehova, anene tsono Israele;


Iwo akukhulupirira Yehova akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.


Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, tinakhala ngati anthu akulota.


Akapanda kumanga nyumba Yehova, akuimanga agwiritsa ntchito chabe; akapanda kusunga mzinda Yehova, mlonda adikira chabe.


Wodala yense wakuopa Yehova, wakuyenda m'njira zake.


Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga, anene tsono Israele;


M'mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.


Yehova, mtima wanga sunadzikuze ndi maso anga sanakwezeke; ndipo sindinatsate zazikulu, kapena zodabwitsa zondiposa.


Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga; ndipo khululukirani zolakwa zanga zonse.


Ndipo Mulungu anamva kubuula kwao, ndi Mulungu anakumbukira chipangano chake ndi Abrahamu, ndi Isaki, ndi Yakobo.


Kumbukirani msauko wanga ndi kusochera kwanga, ndizo chivumulo ndi ndulu.


Yehova, kumbukirani chotigwerachi, penyani nimuone chitonzo chathu.