Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 130:3 - Buku Lopatulika

Mukasunga mphulupulu, Yehova, adzakhala chilili ndani, Ambuye?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mukasunga mphulupulu, Yehova, adzakhala chilili ndani, Ambuye?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, mukadaŵerengera machimo, ndani akadakhala chilili opanda mlandu, Ambuye?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Inu Yehova, mukanamawerengera machimo, Inu Yehova, akanayima chilili ndani wopanda mlandu?

Onani mutuwo



Masalimo 130:3
14 Mawu Ofanana  

Yehova Mulungu wa Israele, Inu ndinu wolungama, popeza tinatsala opulumuka monga lero lino; taonani, tili pamaso panu m'kupalamula kwathu; pakuti palibe wakuima pamaso panu chifukwa cha ichi.


Ndikachimwa mundipenya; ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.


Munthu nchiyani kuti akhale woyera, wobadwa ndi mkazi kuti akhale wolungama?


Chinkana ndikhala wolungama, pakamwa panga padzanditsutsa; chinkana ndikhala wangwiro, padzanditsutsa wamphulupulu.


Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu; pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.


Inu ndinu woopsa; ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala chilili ndani pamaso panu?


Tonse tasochera ngati nkhosa; tonse tayenda yense m'njira ya mwini yekha; ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.


Adzaima ndani pa kulunda kwake? Ndipo adzakhalitsa ndani pa mkwiyo wake wotentha? Ukali wake utsanulidwa ngati moto, ndi matanthwe asweka ndi Iye.


Koma ndani adzapirira tsiku la kudza kwake? Ndipo adzaima ndani pooneka Iye? Pakuti adzanga moto wa woyenga, ndi sopo wa otsuka;


Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isaki, ndi Yakobo; musapenyerera kupulukira kwa anthu awa, kapena choipa chao, kapena tchimo lao;


chifukwa lafika tsiku lalikulu la mkwiyo wao, ndipo akhoza kuima ndani?