Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 128:6 - Buku Lopatulika

Inde, udzaona zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israele.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Inde, udzaona zidzukulu zako. Mtendere ukhala ndi Israele.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ukhale ndi moyo wautali kuti uwone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israele.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

Onani mutuwo



Masalimo 128:6
7 Mawu Ofanana  

Ndipo Israele anati kwa Yosefe, Sindinaganizira kuti ndiona nkhope yako: ndipo, taona, Mulungu wandionetsa ine mbeu zako zomwe.


Ndipo Yosefe anaona ana a Efuremu a mbadwo wachitatu; ananso a Makiri mwana wamwamuna wa Manase anabadwa pa maondo a Yosefe.


Ndipo zitatha izi, Yobu anakhala ndi moyo zaka zana limodzi mphambu makumi anai, naona ana ake ndi zidzukulu zake mibadwo inai.


Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota, Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake. Mtendere ukhale pa Israele.


Zidzukulu ndizo korona wa okalamba; ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.


Pakuti atero Yehova, Taonani ndidzamfikitsira mtendere ngati mtsinje, ndi ulemerero wa amitundu ngati mtsinje wosefukira. Inu mudzayamwa, ndi kunyamulidwa pambali, ndi kululuzidwa pa maondo.


kuti avumbulutse Mwana wake mwa ine, kuti ndimlalikire Iye mwa amitundu; pomwepo sindinafunsane ndi thupi ndi mwazi: