Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 122:9 - Buku Lopatulika

Chifukwa cha nyumba ya Yehova Mulungu wathu ndidzakufunira zokoma.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chifukwa cha nyumba ya Yehova Mulungu wathu ndidzakufunira zokoma.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chifukwa cha Nyumba ya Chauta, Mulungu wathu, ndidzakupemphera zabwino.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

Onani mutuwo



Masalimo 122:9
11 Mawu Ofanana  

Ndiponso popeza ndikondwera nayo nyumba ya Mulungu wanga, chuma changachanga cha golide ndi siliva ndili nacho ndichipereka kunyumba ya Mulungu wanga, moonjezera ndi zonse ndazikonzeratu nyumba yopatulikayo;


Mundikumbukire Mulungu wanga mwa ichi, nimusafafanize zokoma zanga ndinazichitira nyumba ya Mulungu wanga, ndi maudikiro ake.


Atamva Sanibalati Muhoroni, ndi Tobiya kapoloyo Mwamoni, chidawaipira kwakukulu, kuti wadza munthu kuwafunira ana a Israele chokoma.


Pakuti Mordekai Myuda anatsatana naye mfumu Ahasuwero, nakhala wamkulu mwa Ayuda, navomerezeka mwa unyinji wa abale ake wakufunira a mtundu wake zokoma, ndi wakunena za mtendere kwa mbeu yake yonse.


Yehova, ndikonda chikhalidwe cha nyumba yanu, ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.


Pakuti changu cha pa nyumba yanu chandidya; ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.


Pakuti tsiku limodzi m'mabwalo anu likoma koposa masiku ambirimbiri akukhala pena. Kukhala ine wapakhomo m'nyumba ya Mulungu wanga, kundikonda ine koposa kugonera m'mahema a choipa.


Ophunzira ake anakumbukira kuti kunalembedwa, Changu cha pa nyumba yanu chandidya ine.