Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 122:4 - Buku Lopatulika

Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova; akhale mboni ya kwa Israele, Ayamike dzina la Yehova.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova; akhale mboni ya kwa Israele, Ayamike dzina la Yehova.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kumeneko kumapita mafuko onse, anthu ake a Chauta, monga momwe adalamulira Israele kuti akayamike dzina la Chauta.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.

Onani mutuwo



Masalimo 122:4
16 Mawu Ofanana  

Lowani kuzipata zake ndi chiyamiko, ndi kumabwalo ake ndi chilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lake.


Nditsegulireni zipata za chilungamo; ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.


pakuti Yehova anasankha Ziyoni; analikhumba likhale pokhala pake; ndi kuti,


koma anasankha fuko la Yuda, Phiri la Ziyoni limene analikonda.


Ndinamchotsera katundu paphewa pake, manja ake anamasuka ku chotengera.


Monga Yehova analamula Mose, momwemo Aroni anauika patsogolo pa Mboni, usungikeko.


Katatu m'chaka amuna onse azioneka pamaso pa Ambuye Yehova.


Ndipo Mose anatembenuka, natsika m'phirimo, magome awiri a mboni ali m'dzanja lake; magome olembedwa kwina ndi kwina; analembedwa mbali ina ndi inzake yomwe.


Pamenepo padzakhala malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lake, kumeneko muzibwera nazo zonse ndikuuzanizi; nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zophera, magawo anu onse a magawo khumi, ndi nsembe yokweza dzanja lanu, ndi zowinda zanu zosankhika zimene muzilonjezera Yehova.


Koma kumalo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha mwa mafuko anu onse kuikapo dzina lake, ndiko ku chokhalamo chake, muzifunako, ndi kufikako;


Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'malo amene Iye adzasankha, katatu m'chaka; pa chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa, pa chikondwerero cha masabata, ndi pa chikondwerero cha Misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;