Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 120:6 - Buku Lopatulika

Moyo wanga unakhalitsa nthawi pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Moyo wanga unakhalitsa nthawi pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndakhala nthaŵi yaitali pakati pa anthu odana ndi mtendere.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.

Onani mutuwo



Masalimo 120:6
6 Mawu Ofanana  

Moyo wanga uli pakati pa mikango; ndigona pakati pa oyaka moto, ndiwo ana a anthu amene mano ao ali nthungo ndi mivi, ndipo lilime lao ndilo lupanga lakuthwa.


Ndipo iwe, wobadwa ndi munthu iwe, usawaopa, kapena kuopa mau ao; ingakhale mitungwi ndi minga ikhala ndi iwe, nukhala pakati pa zinkhanira, usaopa mau ao kapena kuopsedwa ndi nkhope zao; pakuti ndiwo nyumba yopanduka.


Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu; chifukwa chake khalani ochenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.


ndipo apabanja ake a munthu adzakhala adani ake.


Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akuchitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundumitundu, okhala m'dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzake.