Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 118:18 - Buku Lopatulika

Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kulanga anandilangadi Yehova: koma sanandipereke kuimfa ai.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta wandilanga koopsa, koma sadandisiye kuti ndife.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.

Onani mutuwo



Masalimo 118:18
14 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake tsono lupanga silidzachoka pa nyumba yako nthawi zonse, popeza unandipeputsa Ine, nudzitengera mkazi wa Uriya Muhiti akhale mkazi wako.


Adzakuombola kuimfa m'njala, ndi kumphamvu ya lupanga m'nkhondo.


Ndinatsikira kumatsinde a mapiri, mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha; koma munandikwezera moyo wanga kuuchotsa kuchionongeko, Yehova Mulungu wanga.


Koma poweruzidwa, tilangidwa ndi Ambuye, kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi dziko lapansi.


monga osadziwika, angakhale adziwika bwino; monga alinkufa, ndipo taonani tili ndi moyo; monga olangika, ndipo osaphedwa;