Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 118:13 - Buku Lopatulika

Kundikankha anandikankha ndikadagwa; koma Yehova anandithandiza.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kundikankha anandikankha ndikadagwa; koma Yehova anandithandiza.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adandikankha kwambiri, kotero kuti ndinali pafupi kugwa, koma Chauta adandithandiza.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.

Onani mutuwo



Masalimo 118:13
11 Mawu Ofanana  

Anandisautsa kawirikawiri kuyambira ubwana wanga; koma sanandilake.


Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa; ndisungeni kwa munthu wachiwawa; kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.


Mundichitire chizindikiro choti chabwino; kuti ondida achione, nachite manyazi, popeza Inu, Yehova, munandithandiza ndi kundisangalatsa.


Usandiseka, mdani wangawe; pakugwa ine ndidzaukanso; pokhala ine mumdima Yehova adzakhala kuunika kwanga.


Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi;


Ndipo Davide analumbiranso nati, Atate wako adziwatu kuti wandikomera mtima; nati, Yonatani asadziwe ichi, kuti angamve chisoni; koma pali Yehova, ndiponso pali moyo wako, pakati pa ine ndi imfa pali ngati phazi limodzi.


Ngakhale anauka anthu kukulondolani, ndi kufuna moyo wanu, koma moyo wa mbuye wanga udzamangika m'phukusi la amoyo lakukhala ndi Yehova Mulungu wanu; koma Iye adzaponya miyoyo ya adani anu kuwataya monga chotuluka m'choponyera mwala.