Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 114:4 - Buku Lopatulika

Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo, timapiri ngati anaankhosa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo, timapiri ngati anaankhosa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mapiri aakulu adalumphalumpha ngati nkhosa zamphongo, nazonso zitunda zidalumpha ngati anaankhosa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.

Onani mutuwo



Masalimo 114:4
14 Mawu Ofanana  

Pamenepo linagwedezeka, ndi kutenthemera dziko lapansi, ndi maziko a mapiri ananjenjemera nagwedezeka, pakuti anakwiya Iyeyo.


Aitumphitsa monga mwanawang'ombe; Lebanoni ndi Sirioni monga msona wa njati.


Indedi munthu ayenda ngati mthunzi; Indedi avutika chabe: Asonkhanitsa chuma, ndipo sadziwa adzachilandira ndani?


Muchitiranji nsanje mapiri inu a mitumitu, ndi phirilo Mulungu analikhumba, akhaleko? Inde, Yehova adzakhalabe komweko kosatha.


Ndipo phiri la Sinai linafuka monsemo, popeza Yehova anatsikira m'moto pamenepo; ndi utsi wake unakwera ngati utsi wa m'ng'anjo, ndi phiri lonse linagwedezeka kwambiri.


Ndipo anthu onse anaona mabingu ndi zimphezi, ndi liu la lipenga ndi phiri lilikufuka; ndipo pamene anthu anaziona, ananjenjemera, naima patali.


Mapiri agwedezeka chifukwa cha Iye, ndi zitunda zisungunuka; ndi dziko lapansi likwezeka pamaso pake, ndi maiko ndi onse okhala m'mwemo.


Anaimirira, nandengulitsa dziko lapansi; anapenya, nanjenjemeretsa amitundu; ndi mapiri achikhalire anamwazika, zitunda za kale lomwe zinawerama; mayendedwe ake ndiwo a kale lomwe.


Kodi Yehova anaipidwa nayo mitsinje? Mkwiyo wanu unali pamitsinje kodi, kapena ukali wanu panyanja, kuti munayenda pa akavalo anu, pa magaleta anu a chipulumutso?


Ndipo ndinaona, mpando wachifumu waukulu woyera, ndi Iye wakukhalapo, amene dziko ndi m'mwamba zinathawa pamaso pake, ndipo sanapezedwe malo ao.