Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 113:9 - Buku Lopatulika

Asungitsa nyumba mkazi wosaona mwana, akhale mai wokondwera ndi ana. Aleluya.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Asungitsa nyumba mkazi wosaona mwana, akhale mai wokondwera ndi ana. Aleluya.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Amapatsa banja mkazi wosabala, namsandutsa mai wosangalala wa ana. Tamandani Chauta!

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

Onani mutuwo



Masalimo 113:9
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Isaki anampembedzera mkazi wake kwa Yehova popeza anali wouma: ndipo Yehova analola kupembedza kwake, ndipo Rebeka mkazi wake anatenga pakati.


Ndipo mkaziyo anaima, naona mwana wamwamuna nyengo yomweyo chaka chimene chija Elisa adanena naye.


Mulungu amangitsira banja anthu a pa okha; atulutsa am'ndende alemerere; koma opikisana naye akhala m'dziko lopanda madzi.


Imba, iwe wouma, amene sunabale; imba zolimba ndi kufuula zolimba, iwe amene sunabale mwana; pakuti ana a mfedwa achuluka koposa ana a mkazi wokwatibwa ndi mwamuna, ati Yehova.


Koma ngati mkazi sanadetsedwe, nakhala woyera, pamenepo adzapulumuka, nadzaima.


Pakuti kwalembedwa, Kondwera, chumba iwe wosabala; imba nthungululu, nufuule iwe wosamva kuwawa kwa kubala; pakuti ana ake a iye ali mbeta achuluka koposa ana a iye ali naye mwamuna.


Amene anakhuta anakasuma chakudya; koma anjalawo anachira; inde chumba chabala asanu ndi awiri; ndipo iye amene ali ndi ana ambiri achita liwondewonde.