Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 112:6 - Buku Lopatulika

Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse; wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse; wolungama adzakumbukika ku nthawi yosatha.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pakuti munthu wochita chilungamo sadzagwedezeka konse, sadzaiŵalika mpaka muyaya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.

Onani mutuwo



Masalimo 112:6
13 Mawu Ofanana  

Ndipo ndinauza Alevi kuti adziyeretse, nabwere, nasunge pazipata kupatula tsiku la Sabata. Mundikumbukire ichinso, Mulungu wanga, ndi kundileka monga mwa chifundo chanu chachikulu.


ndi chopereka cha nkhuni pa nthawi zoikika, ndi wa zipatso zoyamba. Mundikumbukire, Mulungu wanga, chindikomere.


Iwo akukhulupirira Yehova akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.


Ndalama zake sakongoletsa mofuna phindu lalikulu, ndipo salandira chokometsera mlandu kutsutsa wosachimwa. Munthu wakuchita izi sadzagwedezeka kunthawi zonse.


Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iye adzakugwiriziza, nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.


Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira kudzenje la chionongeko. Anthu okhetsa mwazi ndi achinyengo masiku ao sadzafikira nusu; koma ine ndidzakhulupirira Inu.


Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukulu.


Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa, msanje wanga, sindidzagwedezeka.


Wolungama sadzachotsedwa konse; koma oipa sadzakhalabe m'dziko.


Amayesa wolungama wodala pomkumbukira; koma dzina la oipa lidzavunda.


pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala ntchito yanu, ndi chikondicho mudachionetsera kudzina lake, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.