Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 110:5 - Buku Lopatulika

Ambuye padzanja lamanja lako adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova pa dzanja lamanja lako adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ambuye ali pambali pako. Adzaphwanya mafumu pa tsiku la mkwiyo wao.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ambuye ali kudzanja lako lamanja; Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.

Onani mutuwo



Masalimo 110:5
23 Mawu Ofanana  

Ichi chikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova, ndi ya iwo akunenera choipa moyo wanga.


Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani padzanja lamanja langa, kufikira nditaika adani anu chopondapo mapazi anu.


Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse; popeza ali padzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.


Pamene Wamphamvuyonse anabalalitsa mafumu m'dzikomo, munayera ngati matalala mu Zalimoni.


Dzudzulani chilombo cha m'bango, khamu la mphongo ndi ng'ombe za anthu, yense wakudzigonjera ndi ndalama za siliva; anabalalitsa mitundu ya anthu ya kukondwera nayo nkhondo.


Munaponda dziko ndi kulunda, munapuntha amitundu ndi mkwiyo.


Pamenepo Ambuye Yesu, atatha kulankhula nao, analandiridwa Kumwamba, nakhala padzanja lamanja la Mulungu.


Koma kolingana ndi kuuma kwako, ndi mtima wako wosalapa, ulikudziunjikira wekha mkwiyo pa tsiku la mkwiyo ndi la kuvumbulutsa kuweruza kolungama kwa Mulungu;


Ndipo amitundu anakwiya, ndipo unadza mkwiyo wanu, ndi nthawi ya akufa yakuti aweruzidwe, ndi yakupereka mphotho akapolo anu aneneriwo, ndi oyera mtima, ndi iwo akuopa dzina lanu, ang'ono ndi akulu; ndi kuononga iwo akuononga dziko.