Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 109:25 - Buku Lopatulika

Ndiwakhaliranso chotonza; pakundiona apukusa mutu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndiwakhaliranso chotonza; pakundiona apukusa mutu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ondineneza amandinyodola, akandiwona amapukusa mitu yao.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.

Onani mutuwo



Masalimo 109:25
13 Mawu Ofanana  

Inenso ndikadanena monga inu, moyo wanu ukadakhala m'malo mwa moyo wanga, ndikadalumikizanitsa mau akutsutsana nanu, ndi kukupukusirani mutu wanga.


Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa, amlanditse tsopano popeza akondwera naye.


awa ndiwo mau amene Yehova wanena za iye, Namwali, mwana wamkazi wa Ziyoni, wakunyoza iwe ndi kuseka iwe ndi chiphwete; mwana wamkazi wa Yerusalemu wapukusa mutu wake pambuyo pako.


Ndipo iwo akupitirirapo anamchitira mwano, napukusa mitu yao, nanena, Ha! Iwe wakupasula Kachisi, ndi kummanga masiku atatu,


Pakuti Khristunso sanadzikondweretse yekha; koma monga kwalembedwa, Minyozo ya iwo amene anakunyoza iwe inagwa pa Ine.


Yesu, ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choikidwacho pamaso pake, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu.


Chifukwa chake titulukire kwa Iye kunja kwa tsasa osenza tonzo lake.