Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 109:13 - Buku Lopatulika

Zidzukulu zake zidulidwe; dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Zidzukulu zake zidulidwe; dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zidzukulu zake zithe nkufa, dzina lao lisamvekenso mu mbadwo wachiŵiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.

Onani mutuwo



Masalimo 109:13
17 Mawu Ofanana  

Ndipo kunali, atalowa ufumu wake, nakhala pa mpando wachifumu wake, anawakantha onse a m'nyumba ya Baasa, osamsiyira mwana wamwamuna ndi mmodzi yense, kapena wa abale ake, kapena wa mabwenzi ake.


ana aamuna khumi a Hamani mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalande zofunkha.


Chikumbukiro chake chidzatayika m'dziko, ndipo adzasowa dzina kukhwalala.


Sadzakhala naye mwana kapena chidzukulu mwa anthu a mtundu wake, kapena wina wotsalira kumene anakhalako.


Mudzaziononga zobala zao kuzichotsa padziko lapansi, ndi mbeu zao mwa ana a anthu.


Pakuti anakupangirani choipa, anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.


Pakuti Yehova akonda chiweruzo, ndipo sataya okondedwa ake. Asungika kosatha, koma adzadula mbumba za oipa.


Amayesa wolungama wodala pomkumbukira; koma dzina la oipa lidzavunda.


Atero Yehova, Lembani munthu uyu wopanda ana, munthu wosaona phindu masiku ake; pakuti palibe munthu wa mbeu zake adzaona phindu, ndi kukhala pa mpando wachifumu wa Davide, ndi kulamuliranso mu Yuda.


Lichotsedwerenji dzina la atate wathu pakati pa banja lake, popeza alibe mwana wamwamuna? Tipatseni dziko lathulathu pakati pa abale a atate wathu.


Ndipo kudzali, pamene Yehova Mulungu wanu atakupumulitsirani adani anu onse ozungulira, m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale cholowa chanuchanu, kuti muzifafaniza chikumbutso cha Amaleke pansi pa thambo; musamaiwala.


Yehova sadzamkhululukira, koma pamenepo mkwiyo wa Yehova ndi nsanje yake zidzamfukira munthuyo; ndipo temberero lonse lolembedwa m'buku ili lidzamkhalira; ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pansi pa thambo.


undileke, ndiwaononge, ndi kufafaniza dzina lao pansi pa thambo; ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi waukulu woposa iwo.


Popeza ndinamuuza kuti ndidzaweruza nyumba yake kosatha chifukwa cha zoipa anazidziwa, popeza ana ake anadzitengera temberero, koma iye sanawaletse.