Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 103:7 - Buku Lopatulika

Analangiza Mose njira zake, ndi ana a Israele machitidwe ake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Analangiza Mose njira zake, ndi ana a Israele machitidwe ake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adadziŵitsa Mose njira zake, adaonetsa Aisraele ntchito zake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.

Onani mutuwo



Masalimo 103:7
19 Mawu Ofanana  

ndi Sabata lanu lopatulika munawadziwitsa, nimunawalamulira malamulo, ndi malemba, ndi chilamulo, mwa dzanja la Mose mtumiki wanu;


zodabwitsa m'dziko la Hamu, zoopsa ku Nyanja Yofiira.


Anaonetsera anthu ake mphamvu ya ntchito zake, pakuwapatsa cholowa cha amitundu.


Aonetsa mau ake kwa Yakobo; malemba ake, ndi maweruzo ake kwa Israele.


Munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa, ndi dzanja la Mose ndi Aroni.


Ndipo anaiwala zochita Iye, ndi zodabwitsa zake zimene anawaonetsa.


Anakhazika mboni mwa Yakobo, naika chilamulo mwa Israele, ndizo analamulira atate athu, akazidziwitse ana ao;


Iye analankhula nao mu mtambo woti njo: Iwo anasunga mboni zake ndi malembawa anawapatsa.


Ndipo Yehova anatsikira paphiri la Sinai, pamutu pake paphiri; ndipo Yehova anaitana Mose akwere pamutu paphiri; ndi Mose anakwerapo.


Ndipo anthu onse anavomera pamodzi, nati, Zonse adazilankhula Yehova tidzazichita. Ndipo Mose anabwera nao mau a anthu kwa Yehova.


Ndipo anthu anaima patali, koma Mose anayandikiza ku mdima waukulu kuli Mulungu.


Ndipo tsopano, ngati ndapeza ufulu pamaso panu, mundidziwitsetu njira zanu, kuti ndikudziweni, ndi kuti ndipeze ufulu pamaso panu; ndipo penyani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.


Satero mtumiki wanga Mose; ndiye wokhulupirika m'nyumba mwanga monse.


Ndipo sanaukenso mneneri mu Israele ngati Mose, amene Yehova anadziwana naye popenyana maso;