Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 103:6 - Buku Lopatulika

Yehova achitira onse osautsidwa chilungamo ndi chiweruzo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova achitira onse osautsidwa chilungamo ndi chiweruzo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta amaweruza mwachilungamo onse opsinjidwa amaŵachitira zolungama.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.

Onani mutuwo



Masalimo 103:6
23 Mawu Ofanana  

Popeza adzaima padzanja lamanja la waumphawi, kumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wake.


Chifukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, ndiuka tsopano, ati Yehova; ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo.


ndiye wakuchitira chiweruzo osautsika; ndiye wakupatsa anjala chakudya; Yehova amasula akaidi.


Mafupa anga onse adzanena, Yehova, afanana ndi Inu ndani, wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu, ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?


Pakuti adzapulumutsa waumphawi wofuulayo; ndi wozunzika amene alibe mthandizi.


Adzaweruza ozunzika a mwa anthu, adzapulumutsa ana aumphawi, nadzaphwanya wosautsa.


Ndipo Yehova adzakhala msanje kwa iye wokhalira mphanthi. Msanje m'nyengo za nsautso;


Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wake; koma wochitira wosauka chifundo amlemekeza.


Usasunthe chidziwitso chakale cha m'malire; ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;


Mwa iwe anapepula atate ndi mai, pakati pa iwe anamchitira mlendo momzunza, mwa iwe anazunza ana amasiye, ndi mkazi wamasiye.


Ndipo kapoloyo anati, Ambuye, chimene munachilamulira chachitika, ndipo malo atsalapo.


Koma inu mumanyoza munthu wosauka. Kodi sakusautsani inu achuma, nakukokerani iwowa kumabwalo a milandu?