Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 100:1 - Buku Lopatulika

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Fuulani kwa Chauta ndi chimwemwe, inu maiko onse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Fuwulani kwa Yehova mwachimwemwe, inu dziko lonse lapansi.

Onani mutuwo



Masalimo 100:1
18 Mawu Ofanana  

Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu; ndipo ndidzalemekeza dzina lanu kunthawi za nthawi.


Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima; ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.


Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu; fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.


Mulungu wakwera ndi mfuu, Yehova ndi liu la lipenga.


Fuulirani kwa Mulungu, dziko lonse lapansi.


Dziko lonse lapansi lidzakugwadirani, ndipo lidzakuimbirani; ndzaimbira dzina lanu.


Anthu akondwere, nafuule mokondwera; pakuti mudzaweruza anthu molunjika, ndipo mudzalangiza anthu padziko lapansi.


Imbirani Mulungu, maufumu a dziko lapansi inu; imbirani Ambuye zomlemekeza.


Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi; kuwitsani ndi kufuulira mokondwera; inde, imbirani zomlemekeza.


Imba, mwana wamkazi wa Ziyoni; fuula, Israele; kondwera nusekerere ndi mtima wonse, mwana wamkazi wa Yerusalemu.


Ndipo Yehova adzakhala mfumu ya dziko lonse; tsiku lomwelo Yehova adzakhala Iye yekha, ndi dzina lake ilo lokha.


Ndipo pakuyandikira Iye tsono potsetsereka pake paphiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau aakulu, chifukwa cha ntchito zonse zamphamvu anaziona;


Ndiponso anena, Kondwani, amitundu inu, pamodzi ndi anthu ake.


Kondwerani, amitundu inu, ndi anthu ake; adzalipsira mwazi wa atumiki ake, adzabwezera chilango akumuukira, nadzafafanizira zoipa dziko lake, ndi anthu ake.