Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 10:11 - Buku Lopatulika

Anena m'mtima mwake, Mulungu waiwala; wabisa nkhope yake; sapenya nthawi zonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Anena m'mtima mwake, Mulungu waiwala; wabisa nkhope yake; sapenya nthawi zonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mumtima mwake amaganiza kuti, “Mulungu sasamalako, waphimba maso ake, sadzaziwona zimenezi.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

Onani mutuwo



Masalimo 10:11
13 Mawu Ofanana  

Ati mumtima mwake, Sindidzagwedezeka ine; ku mibadwomibadwo osagwa m'tsoka ine.


Koma Inu, Yehova, mudzawaseka; mudzalalatira amitundu onse.


Alimbikitsana m'chinthu choipa; apangana za kutchera misampha mobisika; akuti, Adzaiona ndani?


Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi mpaka kutha; chingakhale cha m'kati mwake mwa munthu, ndi mtima wozama.


Namati, Akachidziwa bwanji Mulungu? Kodi Wam'mwambamwamba ali nayo nzeru?


Ndipo amati, Yehova sachipenya, ndi Mulungu wa Yakobo sachisamalira.


Popeza sambwezera choipa chake posachedwa atamtsutsa munthu, ana a anthu atsimikizadi mitima yao kuchita zoipa.


Pamenepo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, wapenya kodi chochita akulu a nyumba ya Israele mumdima, aliyense m'chipinda chake cha zifanizo? Pakuti ati, Yehova satipenya, Yehova wataya dziko.


Pamenepo ananena nane, Mphulupulu ya nyumba ya Israele ndi Yuda ndi yaikulukulu ndithu, ndi dziko ladzala ndi mwazi, ndi mzindawo wadzala ndi kukhotetsa milandu; pakuti ati, Yehova wataya dziko, Yehova sapenya.


Ndipo sanena m'mtima mwao kuti Ine ndikumbukira zoipa zao zonse; tsopano machitidwe ao awazinga; ali pamaso panga.


Koma anakhalapo ena a alembi akuganizira mumtima mwao,


Koma Mfarisi, amene adamuitana Iye, pakuona, ananena mwa yekha, nati, Akadakhala mneneri uyu akadazindikira ali yani, ndi wotani mkaziyo womkhudza Iye, chifukwa ali wochimwa.