Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 9:4 - Buku Lopatulika

Ndipo anaonekera kwa iwo Eliya ndi Mose, alikulankhulana ndi Yesu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anaonekera kwa iwo Eliya ndi Mose, alikulankhulana ndi Yesu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nthaŵi yomweyo ophunzira aja adaona Eliya ndi Mose, akukambirana ndi Yesu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.

Onani mutuwo



Marko 9:4
15 Mawu Ofanana  

Pakuti aneneri onse ndi chilamulo chinanenera kufikira pa Yohane.


ndipo zovala zake zinakhala zonyezimira, zoyera mbuu; monga ngati muomba wotsuka nsalu padziko lapansi sangathe kuziyeretsai.


Ndipo Petro anayankha, nanena ndi Yesu, Rabi, kutikomera ife kukhala pano; ndipo timange misasa itatu; umodzi wa inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya.


Ndipo anayamba kwa Mose, ndi kwa aneneri onse nawatanthauzira iwo m'malembo onse zinthu za Iye yekha.


Ndipo anati kwa iwo, Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m'chilamulo cha Mose, ndi aneneri, ndi Masalimo.


Ndipo anayankha nati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndi ena, kuti anauka mmodzi wa aneneri akale.


Musanthula m'malembo, popeza muyesa kuti momwemo muli nao moyo wosatha; ndipo akundichitira Ine umboni ndi iwo omwewo;


Ndipo ndinagwa pa mapazi ake kumlambira iye. Ndipo ananena ndi ine, Tapenya, usatero; ine ndine kapolo mnzako, ndi mnzao wa abale ako akukhala nao umboni wa Yesu; lambira Mulungu: pakuti umboni wa Yesu ndiwo Mzimu wa chinenero.