Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 6:7 - Buku Lopatulika

Ndipo anadziitanira khumi ndi awiriwo, nayamba kuwatumiza iwo awiriawiri; nawapatsa mphamvu pa mizimu yonyansa;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anadziitanira khumi ndi awiriwo, nayamba kuwatumiza iwo awiriawiri; nawapatsa mphamvu pa mizimu yonyansa;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu adaitana ophunzira ake khumi ndi aŵiri aja, naŵatuma aŵiriaŵiri. Adaŵapatsa mphamvu zotulutsira mizimu yoipitsa anthu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.

Onani mutuwo



Marko 6:7
12 Mawu Ofanana  

Ndipo zizindikiro izi zidzawatsata iwo akukhulupirira: m'dzina langa adzatulutsa ziwanda; adzalankhula ndi malankhulidwe atsopano;


Zitapita izi Ambuye anaika ena makumi asanu ndi awiri, nawatuma iwo awiriawiri pamaso pake kumudzi uliwonse, ndi malo ali onse kumene ati afikeko mwini.


Ndipo ndidzalamulira mboni zanga ziwiri, ndipo zidzanenera masiku chikwi chimodzi ndi mazana awiri amphambu makumi asanu ndi limodzi, zovala chiguduli.