Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 4:29 - Buku Lopatulika

Pakucha zipatso, pamenepo atenga chisenga, pakuti nthawi yakumweta yafika.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakutcha zipatso, pamenepo atenga chisenga, pakuti nthawi yakumweta yafika.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono mbeuzo zikacha, munthu uja amatenga mpeni wodulira, pakuti nyengo yokolola yafika.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mbewuyo ikangokhwima, amayimweta chifukwa nthawi yokolola yakwana.”

Onani mutuwo



Marko 4:29
9 Mawu Ofanana  

Udzafika kumanda utakalamba, monga abwera nao mtolo wa tirigu m'nyengo yake.


Longani chisenga, pakuti dzinthu dzacha; idzani, pondani, pakuti chadzala choponderamo mphesa; zosungiramo zisefuka; pakuti zoipa zao nzazikulu.


Kazilekeni zonse ziwiri, zikulire pamodzi kufikira pakututa; ndimo m'nyengo yakututa ndidzauza akututawo, Muyambe kusonkhanitsa namsongole, mummange uyu mitolo kukamtentha, koma musonkhanitse tirigu m'nkhokwe yanga.


Nthaka ibala zipatso zake yokha; uyamba mmera, zitsata ngala, pamenepo maso okhwima m'ngalamo.


Ndipo mngelo wina anatuluka paguwa la nsembe, ndiye wakukhala nao ulamuliro pamoto; nafuula ndi mau aakulu kwa iye wakukhala nacho chisenga chakuthwa, nanena, Tumiza chisenga chako chakuthwa, nudule matsango a munda wampesa wa m'dziko; pakuti mphesa zake zapsa ndithu.