Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 2:4 - Buku Lopatulika

Ndipo pamene sanakhoze kufika kuli Iye, chifukwa cha khamu la anthu, anasasula tsindwi pokhala Iye; ndipo pamene anatha kuliboola, anatsitsa mphasa m'mene alinkugonamo wodwala manjenjeyo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pamene sanakhoze kufika kuli Iye, chifukwa cha khamu la anthu, anasasula chindwi pokhala Iye; ndipo pamene anatha kuliboola, anatsitsa mphasa m'mene alinkugonamo wodwala manjenjeyo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma sadathe kufika naye pafupi ndi Yesuyo chifukwa cha kuchuluka kwa anthu. Choncho adakwera pa denga, nangosasula dengalo kuyang'anana ndi pamene Yesu analiri, nkutsitsira pachiboopo machira amene adaanyamulira munthu uja.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.

Onani mutuwo



Marko 2:4
3 Mawu Ofanana  

Ndipo mbiri yake inabuka ku Siriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundumitundu, ndi ogwidwa ndi ziwanda, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawachiritsa.


Ndipo posapeza polowa naye, chifukwa cha unyinji wa anthu, anakwera pamwamba pa tsindwi, namtsitsira iye poboola pa tsindwi ndi kama wake, namfikitsa pakati pomwe pamaso pa Yesu.


Pamene mumanga nyumba yatsopano, muzimanga kampanda pa tsindwi lake, kuti ungatengere nyumba yanu mwazi, akagwako munthu.