Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 16:13 - Buku Lopatulika

Ndipo iwowa anachoka nawauza otsala; koma iwo omwe sanawavomereze.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo iwowa anachoka nawauza otsala; koma iwo omwe sanawavomereze.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ophunzirawo adabwerera kudzauza anzao aja, koma iwonso sadaŵakhulupirire.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.

Onani mutuwo



Marko 16:13
9 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene anamuona Iye, anamlambira; koma ena anakayika.


Ndipo iwowo, pamene anamva kuti ali moyo, ndi kuti adapenyeka kwa iye, sanamvere.


Ndipo chitatha icho anaonekera kwa khumi ndi mmodzi iwo okha, alikuseama pachakudya; ndipo anawadzudzula chifukwa cha kusavomereza kwao ndi kuuma mtima, popeza sanavomereze iwo amene adamuona, atauka Iye.


Koma anati kwa iye, Ngati samvera Mose ndi aneneri, sadzakopeka mtima ngakhale wina akauka kwa akufa.


Ndipo mau awa anaoneka pamaso pao ngati nkhani zachabe, ndipo sanamvere akaziwo.


Koma pokhala iwo chikhalire osakhulupirira chifukwa cha chimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, Muli nako kanthu kakudya kuno?


Chifukwa chake ophunzira ena ananena naye, Tamuona Ambuye. Koma iye anati kwa iwo, Ndikapanda kuona m'manja ake chizindikiro cha misomaliyo, ndi kuika chala changa m'chizindikiro cha misomaliyo, ndi kuika dzanja langa kunthiti yake; sindidzakhulupirira.


Pamenepo tsono analowanso wophunzira winayo, amene anayamba kufika kumanda, ndipo anaona, nakhulupirira.