Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 15:10 - Buku Lopatulika

Pakuti anazindikira kuti ansembe aakulu anampereka Iye mwanjiru.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti anazindikira kuti ansembe aakulu anampereka Iye mwanjiru.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adaatero chifukwa adaadziŵa kuti Yesuyo akulu a ansembewo angodzampereka chifukwa cha kaduka chabe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

podziwa kuti akulu a ansembe anamupereka Yesu kwa iye chifukwa cha nsanje.

Onani mutuwo



Marko 15:10
13 Mawu Ofanana  

Ndipo abale ake anamchitira iye nsanje, koma atate wake anasunga mau amene m'mtima mwake.


Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka; koma ndani angalakike ndi nsanje?


Ndiponso ndinapenyera mavuto onse ndi ntchito zonse zompindulira bwino, kuti chifukwa cha zimenezi anansi ake achitira munthu nsanje. Ichinso ndi chabe ndi kungosautsa mtima.


Pakuti anadziwa kuti anampereka Iye mwanjiru.


Koma ansembe aakulu anasonkhezera khamulo, kuti makamaka awamasulire Barabasi.


Ndipo Pilato anawayankha, nanena nao, Kodi mufuna kuti ndikumasulireni mfumu ya Ayuda?


Koma Ayuda, pakuona makamu a anthu, anadukidwa, natsutsana nazo zolankhulidwa ndi Paulo, nachita mwano.


Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akuchitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundumitundu, okhala m'dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzake.


Kodi muyesa kapena kuti malembo angonena chabe? Kodi Mzimuyo adamkhalitsa mwa ife akhumbitsa kuchita nsanje?


osati monga Kaini anali wochokera mwa woipayo, namupha mbale wake. Ndipo anamupha Iye chifukwa ninji? Popeza ntchito zake zinali zoipa, ndi za mbale wake zolungama.