Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 14:8 - Buku Lopatulika

Iye wachita chimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Iye wachita chimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Iyeyu wachita zimene akadatha kuchita. Wadzozeratu thupi langa ndi mafuta onunkhira, kuti alikonzeretu lisanaikidwe m'manda.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wachita zimene akanatha. Wathira mafuta onunkhira pa thupi langa nthawi isanakwane kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.

Onani mutuwo



Marko 14:8
14 Mawu Ofanana  

Anthu anu adzadzipereka eni ake tsiku la chamuna chanu: M'moyera mokometsetsa, mobadwira matanda kucha, muli nao mame a ubwana wanu.


Pakuti mkaziyo, m'mene anathira mafuta awa pathupi panga, wandichitiratu ichi pa kuikidwa kwanga.


Ndipo atafika tsono madzulo, popeza mpa tsiku lokonzekera, ndilo la pambuyo pa Sabata,


Ndipo anautsitsa, naukulunga m'nsalu yabafuta, nauika m'manda osemedwa m'mwala, m'menemo sanaike munthu ndi kale lonse.


Pamenepo Yesu anati, Mleke iye, pakuti anachisungira ichi tsiku la kuikidwa kwanga.


Pakuti ngati chivomerezocho chili pomwepo, munthu alandiridwa monga momwe ali nacho, si monga chimsowa.