Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 14:2 - Buku Lopatulika

pakuti anati, Pachikondwerero ai, kuti pangakhale phokoso la anthu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

pakuti anati, Pachikondwerero ai, kuti pangakhale phokoso la anthu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ankati, “Zimenezi tisadzachite pa nthaŵi ya chikondwerero ai, pangadzachitike chipolowe pakati pa anthu.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anati, “Koma osati nthawi yaphwando, chifukwa anthu angachite chiwawa.”

Onani mutuwo



Marko 14:2
13 Mawu Ofanana  

Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu; koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.


Kulibe nzeru ngakhale luntha ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.


Nkokoma kuti munthu asenze goli ali wamng'ono.


Mudziwa kuti akapita masiku awiri, Paska afika, ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kupachikidwa pamtanda.


Koma ananena iwo, pa nthawi ya chikondwerero iai, kuti pasakhale phokoso la anthu.


Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, chifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.


Koma tikati, Kwa anthu, anaopa anthuwo; pakuti onse anamuyesa Yohane mneneri ndithu.


Ndipo popita masiku awiri kuli phwando la Paska ndi Mkate wopanda chotupitsa; ndipo ansembe aakulu ndi alembi anafunafuna momchitira chiwembu, ndi kumupha:


Ndipo pakukhala Iye ku Betaniya m'nyumba ya Simoni wakhate, m'mene anaseama kudya, anadzapo mkazi ali nayo nsupa ya alabastero ya mafuta onunkhira bwino a narido weniweni a mtengo wapatali; naswa nsupayo, nawatsanulira pamutu pake.


Ndiponso, tikanena, Uchokera kwa anthu; anthu onse adzatiponya miyala: pakuti akopeka mtima, kuti Yohane ali mneneri.


Ndipo chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa chinayandikira, ndicho chotchedwa Paska.


Chifukwa chake Afarisi ananena wina ndi mnzake, Muona kuti simupindula kanthu konse; onani dziko litsata pambuyo pake pa Iye.


Pamenepo ena a khamulo pakumva mau awa, ananena, Mneneriyo ndi uyu ndithu.