Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 11:11 - Buku Lopatulika

Ndipo Iye analowa mu Yerusalemu, mu Kachisi; ndipo m'mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Iye analowa m'Yerusalemu, m'Kachisi; ndipo m'mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu ataloŵa m'Yerusalemu, adakaloŵa m'Nyumba ya Mulungu, nayang'anayang'ana zonse. Tsono poti chisisira chinali chitagwa, adatuluka napita ku Betaniya pamodzi ndi ophunzira ake khumi ndi aŵiri aja.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesu analowa mu Yerusalemu napita ku Nyumba ya Mulungu. Anayangʼana zonse, koma popeza kuti nthawi inali itapita, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

Onani mutuwo



Marko 11:11
8 Mawu Ofanana  

Ndipo anati kwa ine, Lowa, kapenye zonyansa zoipa alikuzichita komweko.


Ndipo kudzachitika nthawi yomweyi kuti ndidzasanthula Yerusalemu ndi nyali, ndipo ndidzalanga amunawo okhala ndi nsenga, onena m'mtima mwao, Yehova sachita chokoma, kapena kuchita choipa.


Taonani, ndituma mthenga wanga, kuti akonzeretu njira pamaso panga; ndipo Ambuye amene mumfuna adzadza ku Kachisi wake modzidzimutsa; ndiye mthenga wa chipangano amene mukondwera naye; taonani akudza, ati Yehova wa makamu.


Ndipo masiku onse madzulo anatuluka Iye m'mzinda.