Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 11:10 - Buku Lopatulika

Wolemekezeka Ufumu ulinkudza, wa atate wathu Davide; Hosana mu Kumwambamwamba.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Wolemekezeka Ufumu ulinkudza, wa atate wathu Davide; Hosana m'Kumwambamwamba.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Udalitsidwe Ufumu wa atate athu Davide umene ulikudza tsopano. Ulemu kwa Mulungu kumwambamwamba.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Odala ndi ufumu umene ukubwera wa abambo athu Davide!” “Hosana Mmwambamwamba!”

Onani mutuwo



Marko 11:10
13 Mawu Ofanana  

Aleluya. Lemekezani Yehova kochokera kumwamba; mlemekezeni m'misanje.


pamenepo ndidzatayanso mbeu ya Yakobo, ndi ya Davide mtumiki wanga, kuti sindidzatenganso za mbeu zake kuti zikhale zolamulira mbeu za Abrahamu, ndi za Isaki, ndi za Yakobo; pakuti ndidzabweza undende wao, ndipo ndidzawachitira chifundo.


atatero ana a Israele adzabwera, nadzafuna Yehova Mulungu wao, ndi Davide mfumu yao, nadzafika ndi mantha kwa Yehova, ndi ku ukoma wake masiku otsiriza.


Ndipo mipingo yakumtsogolera ndi yakumtsatira, inafuula, kuti, Hosana kwa Mwana wa Davide! Wolemekezeka ndiye wakudza m'dzina la Ambuye! Hosana mu Kumwambamwamba!


ndipo musamayesa kunena mwa inu nokha, Atate wathu tili naye Abrahamu; pakuti ndinena kwa inu kuti mwa miyala iyi Mulungu akhoza kuukitsira Abrahamu ana.


Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba, ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.