Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 10:41 - Buku Lopatulika

Ndipo pamene khumiwo anamva, anayamba kupsa mtima chifukwa cha Yakobo ndi Yohane.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pamene khumiwo anamva, anayamba kupsa mtima chifukwa cha Yakobo ndi Yohane.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamene khumi ena aja adamva zimenezi, adapsera mtima Yakobeyo ndi Yohaneyo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ophunzira khumiwo otsalawo atamva izi anapsera mtima Yakobo ndi Yohane.

Onani mutuwo



Marko 10:41
9 Mawu Ofanana  

Kudzikuza kupikisanitsa; koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.


Ndipo m'mene khumiwo anamva, anapsa mtima ndi abale awiriwo.


Ndipo Yesu anawaitana, nanena nao, Mudziwa kuti iwo amene ayesedwa ambuye a mitundu ya anthu amachita ufumu pa iwo; ndipo akulu ao amachita ulamuliro pa iwo.


Ndipo kunakhala kutsutsana mwa iwo, ndani wa iwo ayesedwe wamkulu.


Ndipo anati kwa iwo, Mafumu a anthu a mitundu awachitira ufumu; ndipo iwo amene awachitira ulamuliro anenedwa, Ochitira zabwino.


M'chikondano cha anzanu wina ndi mnzake mukondane ndi chikondi chenicheni; mutsogolerane ndi kuchitira wina mnzake ulemu;


musachite kanthu monga mwa chotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pake, komatu ndi kudzichepetsa mtima, yense ayese anzake omposa iye mwini;


Kodi muyesa kapena kuti malembo angonena chabe? Kodi Mzimuyo adamkhalitsa mwa ife akhumbitsa kuchita nsanje?