Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Marko 1:9 - Buku Lopatulika

Ndipo kunali masiku omwewo, Yesu anadza kuchokera ku Nazarete wa ku Galileya, nabatizidwa ndi Yohane mu Yordani.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo kunali masiku omwewo, Yesu anadza kuchokera ku Nazarete wa ku Galileya, nabatizidwa ndi Yohane m'Yordani.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pa masiku amenewo Yesu adafika kuchokera ku Nazarete, mudzi wa ku Galileya, ndipo Yohane adambatiza mu mtsinje wa Yordani.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.

Onani mutuwo



Marko 1:9
7 Mawu Ofanana  

nadza nakhazikika m'mzinda dzina lake Nazarete kuti chikachitidwe chonenedwa ndi aneneri kuti, Adzatchedwa Mnazarayo.


Ndipo pomwepo, alimkukwera potuluka m'madzi, anaona Iye thambo litang'ambika, ndi Mzimu alikutsikira pa Iye monga nkhunda:


Ndakubatizani inu ndi madzi; koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.


Ndipo anatsika nao pamodzi nadza ku Nazarete; nawamvera iwo: ndipo amake anasunga zinthu izi zonse mumtima mwake.


kuyambira ubatizo wa Yohane, kufikira tsiku lija anatengedwa kunka Kumwamba kutisiya ife, mmodzi wa awa akhale mboni ya kuuka kwake pamodzi ndi ife.