Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Machitidwe a Atumwi 8:4 - Buku Lopatulika

Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Okhulupirira amene adabalalika aja adapita m'dziko monse akulalika Uthenga Wabwino.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Okhulupirira amene anabalalika amalalikira konse kumene amapita.

Onani mutuwo



Machitidwe a Atumwi 8:4
8 Mawu Ofanana  

Koma pamene angakuzunzeni inu m'mudzi uwu, thawirani mwina: indetu ndinena kwa inu, Simudzaitha mizinda ya Israele, kufikira Mwana wa Munthu atadza.


monga anazipereka kwa ife iwo amene anakhala mboni ndi atumiki a mau,


Pamenepo iwotu, akubalalika chifukwa cha chisautsocho chidadza pa Stefano, anafikira ku Fenisiya, ndi Kipro, ndi Antiokeya, osalankhula mau kwa wina yense koma kwa Ayuda okha.


Koma Paulo ndi Barnabasi anakhalabe mu Antiokeya, nalinkuphunzitsa, ndi kulalikira mau a Ambuye pamodzi ndi ena ambiri.


Ndipo Saulo analikuvomerezana nao pa imfa yake. Ndipo tsikulo kunayamba kuzunza kwakukulu pa Mpingo unali mu Yerusalemu; ndipo anabalalitsidwa onse m'maiko a Yudeya ndi Samariya, koma osati atumwi ai.


Koma pamene anakhulupirira Filipo wakulalikira Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu ndi dzina la Yesu Khristu, anabatizidwa, amuna ndi akazi.


koma tingakhale tidamva zowawa kale, ndipo anatichitira chipongwe, monga mudziwa, ku Filipi, tinalimbika pakamwa mwa Mulungu wathu kulankhula ndi inu Uthenga Wabwino wa Mulungu m'kutsutsana kwambiri.