Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Machitidwe a Atumwi 7:17 - Buku Lopatulika

Koma m'mene inayandikira nthawi ya lonjezo limene Mulungu adalonjezana ndi Abrahamu, anthuwo anakula nachuluka mu Ejipito,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma m'mene inayandikira nthawi ya lonjezo limene Mulungu adalonjezana ndi Abrahamu, anthuwo anakula nachuluka m'Ejipito,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Pamene idayandikira nthaŵi yakuti Mulungu achite zimene adaalonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu udakula ndi kuchuluka ku Ejipito.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto.

Onani mutuwo



Machitidwe a Atumwi 7:17
8 Mawu Ofanana  

Ndipo Israele anakhala m'dziko la Ejipito, m'dziko la Goseni; nakhala nazo zaozao m'menemo, nabalana nachuluka kwambiri.


Potero Mulungu anawachitira zabwino anamwino; ndipo anthuwo anachuluka, nakhala nazo mphamvu zazikulu.


Mulungu wa anthu awa Israele anasankha makolo athu, nakweza anthuwo pakugonerera iwo m'dziko la Ejipito, ndipo ndi dzanja lokwezeka anawatulutsa iwo m'menemo.


Koma Mulungu analankhula chotero, kuti mbeu yake idzakhala alendo m'dziko la eni, ndipo adzawachititsa ukapolo, nadzawachitira choipa, zaka mazana anai.