Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Machitidwe a Atumwi 7:11 - Buku Lopatulika

Koma inadza njala pa Ejipito ndi Kanani yense, ndi chisautso chachikulu; ndipo sanapeze chakudya makolo athu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma inadza njala pa Ejipito ndi Kanani lonse, ndi chisautso chachikulu; ndipo sanapeza chakudya makolo athu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma mudadzaloŵa njala m'dziko lonse la Ejipito, ndiponso m'Kanani, kotero kuti anthu adazunzika kwambiri. Makolo athu omwe sadathe kupeza chakudya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya.

Onani mutuwo



Machitidwe a Atumwi 7:11
8 Mawu Ofanana  

Ndipo ana aamuna a Israele anadza kudzagula mwa iwo amene anadzako, pakuti m'dziko la Kanani munali njala.


Ndipo njala inakula m'dzikomo.


ndipo ndidzachereza inu komweko; pakuti zatsala zaka zisanu za njala; kuti mungafikire umphawi, inu ndi banja lanu, ndi onse muli nao.


Nati kwa Farao, Tafika kuti tikhale m'dzikomo; popeza palibe podyetsa zoweta za akapolo anu; pakuti njala yakula m'dziko la Kanani. Mulole tsopano akapolo anu akhale m'dziko la Goseni.


Ndipo anaitana njala igwere dziko; anathyola mchirikizo wonse wa mkate.