Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Machitidwe a Atumwi 2:12 - Buku Lopatulika

Ndipo anadabwa onse, nathedwa nzeru, nanena wina ndi mnzake, Kodi ichi nchiyani?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anadabwa onse, nathedwa nzeru, nanena wina ndi mnzake, Kodi ichi nchiyani?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Onse adazizwa ndi kuthedwa nzeru, ndipo adayamba kufunsana kuti, “Kodi chimenechi nchiyani?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”

Onani mutuwo



Machitidwe a Atumwi 2:12
8 Mawu Ofanana  

Ndipo panakhala pamene Yesu anatha mau amenewa, makamu a anthu anazizwa ndi chiphunzitso chake:


pakuti Herode anaopa Yohane, podziwa kuti ali munthu wolungama ndi woyera mtima, ndipo anamsunga iye. Ndipo pamene anamva iye anathedwa nzeru, nakondwa kumva iye.


Ndipo anaitana mmodzi wa anyamata, namfunsa, Zinthu izi nzotani?


ndipo pakumva khamu la anthu alinkupita, anafunsa, Ichi nchiyani?


Ndipo pokayikakayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti chiyani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Kornelio, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pachipata,


Pakuti ufika nazo kumakutu athu zachilendo: tifuna tsono kudziwa, izi zitani?


ndiwo Ayuda, ndiponso opinduka, Akrete, ndi Aarabu, tiwamva iwo alikulankhula m'malilime athu zazikulu za Mulungu.


Ndipo anadabwa onse, nazizwa, nanena, Taonani, awa onse alankhulawa sali Agalileya kodi?