Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Machitidwe a Atumwi 10:8 - Buku Lopatulika

ndipo m'mene adawafotokozera zonse, anawatuma ku Yopa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo m'mene adawafotokozera zonse, anawatuma ku Yopa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kornelio uja ataŵafotokozera zonse, adaŵatuma ku Yopa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anawafotokozera zonse zimene zinachitika ndipo anawatuma kuti apite ku Yopa.

Onani mutuwo



Machitidwe a Atumwi 10:8
11 Mawu Ofanana  

Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.


Ndipo pokayikakayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti chiyani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Kornelio, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pachipata,


Pamenepo ndinatumiza kwa inu osachedwa; ndipo mwachita bwino mwadza kuno. Chifukwa chake taonani tilitonse pano pamaso pa Mulungu, kumva zonse Ambuye anakulamulirani.


Ndipo m'mene atachoka mngelo amene adalankhula naye, anaitana anyamata ake awiri, ndi msilikali wopembedza, wa iwo amene amtumikira kosaleka;


Potero, Mfumu Agripa, sindinakhale ine wosamvera masomphenya a Kumwamba;


Koma mu Yopa munali wophunzira dzina lake Tabita, ndilo kunena Dorika; mkazi ameneyo anadzala ndi ntchito zabwino ndi zachifundo zimene anazichita.


Ndipo popeza Lida ndi pafupi pa Yopa, m'mene anamva ophunzirawo kuti Petro anali pomwepo, anamtumizira anthu awiri, namdandaulira, Musachedwa mudze kwa ife.


Ndipo kudadziwika ku Yopa konse: ndipo ambiri anakhulupirira Ambuye.


Ndipo kunali, kuti anakhala iye mu Yopa masiku ambiri ndi munthu Simoni wofufuta zikopa.


kuti avumbulutse Mwana wake mwa ine, kuti ndimlalikire Iye mwa amitundu; pomwepo sindinafunsane ndi thupi ndi mwazi: