Machitidwe a Atumwi 10:5 - Buku Lopatulika Ndipo tsopano tumiza amuna ku Yopa, aitane munthu Simoni, wotchedwanso Petro; Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo tsopano tumiza amuna ku Yopa, aitane munthu Simoni, wotchedwanso Petro; Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Tsopano tuma anthu ku Yopa kuti akaitane munthu wina, dzina lake Simoni, wotchedwanso Petro. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Tsopano tuma anthu apite ku Yopa kuti akayitane munthu dzina lake Simoni Petro. |
Anadza naye kwa Yesu. M'mene anamyang'ana iye, anati, Uli Simoni mwana wa Yohane; udzatchedwa Kefa (ndiko kusandulika Petro).
Chifukwa chake tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni amene anenedwanso Petro; amene acherezedwa m'nyumba ya Simoni wofufuta zikopa, m'mbali mwa nyanja.
Ndipo pamene panali mafunsano ambiri, Petro anaimirira, nati kwa iwo, Abale, mudziwa kuti poyamba Mulungu anasankha mwa inu, kuti m'kamwa mwanga amitundu amve mau a Uthenga Wabwino, nakhulupirire.
Ndipo masomphenya anaonekera kwa Paulo usiku: Panali munthu wa ku Masedoniya alinkuimirira, namdandaulira kuti, Muolokere ku Masedoniya kuno, mudzatithangate ife.
Koma mu Yopa munali wophunzira dzina lake Tabita, ndilo kunena Dorika; mkazi ameneyo anadzala ndi ntchito zabwino ndi zachifundo zimene anazichita.
Ndipo popeza Lida ndi pafupi pa Yopa, m'mene anamva ophunzirawo kuti Petro anali pomwepo, anamtumizira anthu awiri, namdandaulira, Musachedwa mudze kwa ife.
Ndipo kunali, kuti anakhala iye mu Yopa masiku ambiri ndi munthu Simoni wofufuta zikopa.