Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 8:53 - Buku Lopatulika

Ndipo anamseka Iye pwepwete podziwa kuti anafa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anamseka Iye pwepwete podziwa kuti anafa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamenepo anthuwo adayamba kumseka monyodola, chifukwa ankadziŵa kuti mwanayo wamwalira basi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.

Onani mutuwo



Luka 8:53
11 Mawu Ofanana  

Ndine ngati munthu wosekedwa ndi mnansi wake, ndinaitana kwa Mulungu, ndipo anandiyankha; munthu wolungama wangwiro asekedwa.


Zoonadi, ali nane ondiseka; ndi diso langa lili chipenyere m'kundiwindula kwao.


Onse akundipenya andiseka; akwenzula, apukusa mutu, nati,


Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeze.


ananena, Tulukani, pakuti kabuthuko sikanafe koma kali m'tulo. Ndipo anamseka Iye pwepwete.


Koma Afarisi, ndiwo okonda ndalama, anamva izi zonse; ndipo anamseka.


Ndipo anthu onse analikumlira iye ndi kudziguguda pachifuwa. Koma Iye anati, Musalire; pakuti iye sanafe, koma wagona tulo.


Ndipo Iye anamgwira dzanja lake, naitana, nati, Buthu, tauka.


Yesu ananena, Chotsani mwala. Marita, mlongo wake wa womwalirayo, ananena ndi Iye, Ambuye, adayamba kununkha: pakuti wagona masiku anai.