Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 7:17 - Buku Lopatulika

Ndipo mbiri yake imeneyo inabuka ku Yudeya yense, ndi ku dziko lonse loyandikira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo mbiri yake imeneyo inabuka ku Yudeya lonse, ndi ku dziko lonse loyandikira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mbiri ya Yesuyi idawanda m'dziko lonse la Yudeya, ndi ku madera onse ozungulira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mbiriyi inafalikira ku Yudeya konse ndi ku madera ozungulira.

Onani mutuwo



Luka 7:17
8 Mawu Ofanana  

Ndipo pa kubadwa kwake kwa Yesu mu Betelehemu wa Yudeya m'masiku a Herode mfumu, onani, Anzeru a kum'mawa anafika ku Yerusalemu,


Ndipo mbiri yake inabuka ku Siriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundumitundu, ndi ogwidwa ndi ziwanda, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawachiritsa.


Ndipo mbiri yake imene inabuka m'dziko lonse limenelo.


Koma iwo anatulukamo, nabukitsa mbiri yake m'dziko lonselo.


Ndipo mbiri yake inabuka pompaja kudziko lonse la Galileya lozungulirapo.


Ndipo mfumu Herode anamva izi; pakuti dzina lake lidamveka; ndipo ananena, kuti, Yohane Mbatizi wauka kwa akufa, ndipo chifukwa chake mphamvu izi zichitachita mwa Iye.


Ndipo Yesu anabwera ndi mphamvu ya Mzimu ku Galileya; ndipo mbiri yake ya Iye inabuka ku dziko lonse loyandikira.


Ndipo anayandikira, nakhudza chithatha; ndipo akumnyamulawo anaima. Ndipo Iye anati, Mnyamata iwe, ndinena ndi iwe, Tauka.