Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 5:16 - Buku Lopatulika

Koma Iye anazemba, nanka m'mapululu, nakapemphera.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Iye anazemba, nanka m'mapululu, nakapemphera.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Iye adapita kumalo kosapitapita anthu, namakapemphera kumeneko.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.

Onani mutuwo



Luka 5:16
8 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.


Ndipo atalawirana nao, anachoka Iye, nalowa m'phiri kukapemphera.


Pamene anthu onse anabatizidwa, Yesu nayenso anabatizidwa. Iye anali kupemphera, ndipo kuthambo kunatseguka,


Ndipo kunali masiku awa, Iye anatuluka nanka kuphiri kukapemphera; nachezera usiku wonse m'kupemphera kwa Mulungu.


Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.


Ndipo m'kupemphera kwake, maonekedwe a nkhope yake anasandulika, ndi chovala chake chinayera ndi kunyezimira.


Pamenepo Yesu, pozindikira kuti alikufuna kudza kudzamgwira Iye, kuti amlonge ufumu, anachokanso kunka kuphiri pa yekha.