Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 4:15 - Buku Lopatulika

Ndipo Iye anaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalemekezedwa ndi anthu onse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Iye anaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalemekezedwa ndi anthu onse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ankaphunzitsa m'nyumba zao zamapemphero, ndipo anthu onse ankamutamanda.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.

Onani mutuwo



Luka 4:15
10 Mawu Ofanana  

Taona, iwe udzaitana mtundu umene sunaudziwe, ndi mtundu umene sunakudziwe udzakuthamangira, chifukwa cha Yehova Mulungu wako, ndi chifukwa cha Woyera wa Israele; pakuti Iye wakukometsa.


Ndipo pofika kudziko la kwao, anaphunzitsa iwo m'sunagoge mwao, kotero kuti anazizwa, nanena, Uyu adazitenga kuti nzeru zimenezi ndi zamphamvu izi?


Ndipo Yesu anayendayenda mu Galileya monse, analikuphunzitsa m'masunagoge mwao, nalalikira Uthenga Wabwino wa Ufumu, nachiritsa nthenda zonse ndi kudwala konse mwa anthu.


Ndipo Yesu anayendayenda m'mizinda yonse ndi m'midzi, namaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalalikira Uthenga Wabwino wa Ufumuwo, nachiritsa nthenda iliyonse ndi zofooka zonse.


Ndipo m'mene anthu a makamu anachiona, anaopa, nalemekeza Mulungu, wakupatsa anthu mphamvu yotere.


Ndipo anazizwa onse, kotero kuti anafunsana mwa iwo okha, kuti, Ichi nchiyani? Chiphunzitso chatsopano! Ndi mphamvu alamula ingakhale mizimu yonyansa, ndipo imvera Iye.


Ndipo analowa m'masunagoge mwao mu Galileya monse, nalalikira, natulutsa ziwanda.


Koma iye anatuluka nayamba kulalikira ndithu, ndi kubukitsa mauwo, kotero kuti Yesu sanathe kulowanso poyera m'mudzi, koma anakhala padera m'mapululu; ndipo anadza kwa Iye anthu a kumalo onse.


Ndipo analikuphunzitsa m'sunagoge mwina, tsiku la Sabata.


Ndipo anadza ku Nazarete, kumene analeredwa; ndipo tsiku la Sabata analowa m'sunagoge, monga anazolowera, naimiriramo kuwerenga m'kalata.