Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 23:9 - Buku Lopatulika

Ndipo anamfunsa Iye mau ambiri; koma Iye sanamyankhe kanthu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anamfunsa Iye mau ambiri; koma Iye sanamyankhe kanthu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Herode adamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sadamuyankhe kanthu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.

Onani mutuwo



Luka 23:9
13 Mawu Ofanana  

Ndinakhala duu, sindinatsegule pakamwa panga; chifukwa inu mudachichita.


Iye anatsenderezedwa koma anadzichepetsa yekha osatsegula pakamwa pake; ngati nkhosa yotsogoleredwa kukaphedwa, ndi ngati mwanawankhosa amene ali duu pamaso pa omsenga, motero sanatsegule pakamwa pake.


Ndipo pakumnenera Iye ansembe aakulu ndi akulu, Iye sanayankhe kanthu.


Ndipo sanayankhe Iye, ngakhale mau amodzi, kotero kuti kazembe anazizwa ndithu.


Musamapatsa chopatulikacho kwa agalu, ndipo musamaponya ngale zanu patsogolo pa nkhumba, kuti zingazipondereze ndi mapazi ao, ndi potembenuka zingang'ambe inu.


Koma Yesu sanayankhenso kanthu; kotero kuti Pilato anazizwa.


Ndipo Iye anati kwa iwo, Pitani kauzeni nkhandweyo, Taonani, nditulutsa ziwanda, nditsiriza machiritso lero ndi mawa, ndipo mkucha nditsirizidwa.


Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anaimirira, namnenera Iye kolimba.


Ndipo analowanso ku Pretorio, nanena kwa Yesu, Muchoka kuti? Koma Yesu sanamyankhe kanthu.


Koma palembo pamene analikuwerengapo ndipo: Ngati nkhosa anatengedwa kukaphedwa, ndi monga mwanawankhosa ali duu pamaso pa womsenga, kotero sanatsegule pakamwa pake.


amene pochitidwa chipongwe sanabwezere chipongwe, pakumva zowawa, sanaopse, koma anapereka mlandu kwa Iye woweruza kolungama;