Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 22:10 - Buku Lopatulika

Ndipo Iye anati kwa iwo, Onani, mutalowa m'mzinda, adzakomana ndinu munthu alikusenza mtsuko wa madzi; mumtsate ameneyo kunyumba kumene akalowako iye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Iye anati kwa iwo, Onani, mutalowa m'mudzi, adzakomana ndinu munthu alikusenza mtsuko wa madzi; mumtsate ameneyo kunyumba kumene akalowako iye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu adati, “Mvetsani! Mukangoloŵa m'mudzimu, mukumana ndi munthu wamwamuna atasenza mtsuko wa madzi. Mukamtsatire mpaka kunyumba kumene akaloŵe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe,

Onani mutuwo



Luka 22:10
8 Mawu Ofanana  

si chimene chilowa m'kamwa mwake chiipitsa munthu; koma chimene chituluka m'kamwa mwake, ndicho chiipitsa munthu.


Ndipo mukanene kwa mwini nyumbayo, Mphunzitsi anena nawe, Chipinda cha alendo chili kuti, m'mene ndikadye Paska pamodzi ndi ophunzira anga?


Ndipo iwo ananena naye, Mufuna tikakonzere kuti?


Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanene kwa inu kuyambira pachiyambi, chifukwa ndinali pamodzi ndi inu.