Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 2:47 - Buku Lopatulika

Ndipo onse amene anamva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake, ndi mayankho ake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo onse amene anamva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake, ndi mayankho ake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Onse amene ankamva mau ake, ankadabwa ndi mayankho ake anzeru.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake.

Onani mutuwo



Luka 2:47
13 Mawu Ofanana  

Ndili nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse; pakuti ndilingalira mboni zanu.


Ndipo pofika kudziko la kwao, anaphunzitsa iwo m'sunagoge mwao, kotero kuti anazizwa, nanena, Uyu adazitenga kuti nzeru zimenezi ndi zamphamvu izi?


Ndipo pamene makamu a anthu anamva, anazizwa ndi chiphunzitso chake.


Ndipo panakhala pamene Yesu anatha mau amenewa, makamu a anthu anazizwa ndi chiphunzitso chake:


Ndipo anazizwa ndi chiphunzitso chake; pakuti anaphunzitsa monga mwini mphamvu, si monga alembi.


Ndipo ansembe aakulu ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, chifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.


Ndipo pofika tsiku la Sabata, anayamba kuphunzitsa m'sunagoge; ndipo ambiri anamva Iye, nazizwa, nanena, Uyu adazitenga kuti izi? Nzeru yopatsidwa kwa munthuyu njotani, ndi zamphamvu zotere zochitidwa ndi manja ake?


Ndipo anthu onse amene anamva anazizwa ndi zinthu abusa adalankhula nao.


Ndipo pakupita masiku atatu, anampeza Iye mu Kachisi, analikukhala pakati pa aphunzitsi, namva iwo, nawafunsanso mafunso.


Ndipo onse anamchitira Iye umboni nazizwa ndi mau a chisomo akutuluka m'kamwa mwake; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?


chifukwa mau ake anali ndi ulamuliro.


Chifukwa chake Ayuda anazizwa, nanena, Ameneyu adziwa bwanji zolemba, wosaphunzira?


Anyamatawo anayankha, Nthawi yonse palibe munthu analankhula chotero.