Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 19:41 - Buku Lopatulika

Ndipo m'mene anayandikira, anaona mzindawo naulirira,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo m'mene anayandikira, anaona mudziwo naulirira,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu atayandikira, nkuwona Yerusalemu, adalira chifukwa cha mzindawo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira

Onani mutuwo



Luka 19:41
14 Mawu Ofanana  

Ndipo anamyang'ana chidwi, mpaka anachita manyazi, nalira misozi munthu wa Mulungu.


Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi, popeza sasamalira chilamulo chanu.


Ndinapenya ochita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao; popeza sasamalira mau anu.


Ndinasumwa kwakukulu, chifukwa cha oipa akusiya chilamulo chanu.


Chomwecho ndinati, Usandiyang'ane ine, ndilira ndi kuwawa mtima; usafulumire kunditonthoza ine, chifukwa cha kufunkhidwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.


Pakuti Yehova adzauka monga m'phiri la Perazimu, nadzakwiya monga m'chigwa cha Gibiyoni; kuti agwire ntchito yake, ntchito yake yachilendo, ndi kuti achite chochita chake, chochita chake chachilendo.


Koma ngati simudzamva, moyo wanga udzalira m'tseri chifukwa cha kunyada kwanu; diso langa lidzalira kwambiri, lidzagwa misozi, chifukwa zoweta za Yehova zagwidwa m'nsinga.


Koma ine, pokhala mbusa sindinafulumire kuchokerako kuti ndikutsateni Inu; sindinakhumbe tsiku la tsoka; Inu mudziwa, chimene chinatuluka pa milomo yanga chinali pamaso panu.


Ha, mutu wanga ukadakhala madzi, ndi maso anga kasupe wa misozi, kuti usana ndi usiku ndilirire ophedwa a mwana wamkazi wa anthu anga!


Ndidzakusiya bwanji, Efuremu? Ndidzakupereka bwanji, Israele? Ndidzakuyesa bwanji ngati Adima? Ndidzakuika bwanji ngati Zeboimu? Mtima wanga watembenuka m'kati mwanga, zachifundo zanga zilira zonse pamodzi.


nanena, Ukadazindikira tsiku ili, inde iwetu zinthu za mtendere! Koma tsopano zibisika pamaso pako.