Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 14:9 - Buku Lopatulika

ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndiye iye uja amene adaitana aŵiri nonsenu nkudzakuuza kuti, ‘Pepani, patsani aŵa maloŵa.’ Apo iweyo udzachita manyazi pokakhala pa malo otsika.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika.

Onani mutuwo



Luka 14:9
8 Mawu Ofanana  

Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; koma nzeru ili ndi odzichepetsa.


Kunyada kutsogolera kuonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kuphunthwa.


Anzeru adzalandira ulemu cholowa chao; koma opusa adzakweza manyazi.


Ndipo pamene Iye anatero, onse aja akutsutsana naye ananyazitsidwa; ndipo anthu onse a m'khamu anakondwera ndi zinthu zonse za ulemererozo zinachitidwa ndi Iye.


Chifukwa chake balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tili naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.