Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 12:43 - Buku Lopatulika

Wodala kapoloyo amene mbuye wake pakufika, adzampeza alikuchita chotero.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Wodala kapoloyo amene mbuye wake pakufika, adzampeza alikuchita chotero.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngwodala wantchito ameneyo, ngati mbuye wake pofika adzampeza akuchitadi zimenezi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zidzamukhalira bwino wantchito amene mbuye wake adzamupeza akuchita zimene pamene iye abwera.

Onani mutuwo



Luka 12:43
8 Mawu Ofanana  

Maso anga ayang'ana okhulupirika m'dziko, kuti akhale ndi Ine; iye amene ayenda m'njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.


Wosunga mkuyu adzadya zipatso zake; wosamalira ambuyake adzalemekezedwa.


Wodala munthu amene achita ichi, ndi mwana wa munthu amene agwira zolimba ichi, amene asunga Sabata osaliipitsa, nasunga dzanja lake osachita nalo choipa chilichonse.


Wodala kapolo amene mbuye wake, pakufika, adzampeza iye alikuchita chotero.


Odala akapolowo amene mbuye wao, pakudza iye, adzawapeza odikira; indetu ndinena ndinu, kuti iye adzadzimangira m'chuuno, nadzawakhalitsa pansi kudya, nadzafika, nadzawatumikira.


Ndipo Ambuye anati, Ndani tsono ali mdindo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wake adzamuika kapitao wa pa banja lake, kuwapatsa iwo phoso lao pa nthawi yake?


Ndinena ndinu zoona, kuti adzamuika iye kapitao wa pa zonse ali nazo.


Momwemo, okondedwa, popeza muyembekeza izi, chitani changu kuti mupezedwe ndi Iye mumtendere, opanda banga ndi opanda chilema.