Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 1:29 - Buku Lopatulika

Koma iye ananthunthumira ndi mau awa, nasinkhasinkha kulonjera uku nkutani.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma iye ananthunthumira ndi mau awa, nasinkhasinkha kulonjera uku nkutani.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Maria adadzidzimuka nawo kwambiri mau ameneŵa, nayamba kusinkhasinkha kuti kodi moni umenewu ndi wa mtundu wanji?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.

Onani mutuwo



Luka 1:29
12 Mawu Ofanana  

Ndipo iwo anafunsana wina ndi mnzake, nati, Sitinatenge mikate.


Ndipo Zekariya anadabwa pamene anamuona, ndipo mantha anamgwira.


Ndipo pakulowa mngelo anati kwa iye, Tikuoneni, wochitidwa chisomo, Ambuye ali ndi iwe.


Ndipo onse amene anazimva anazisunga m'mtima mwao, nanena, Nanga mwana uyu adzakhala wotani? Pakuti dzanja la Ambuye linakhala pamodzi ndi iye.


Koma Maria anasunga mau awa onse, nawalingalira mumtima mwake.


Ndipo anatsika nao pamodzi nadza ku Nazarete; nawamvera iwo: ndipo amake anasunga zinthu izi zonse mumtima mwake.


Ndipo pokayikakayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti chiyani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Kornelio, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pachipata,


Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nchiyani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zachifundo zako zinakwera zikhala chikumbutso pamaso pa Mulungu.