Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Hoseya 7:9 - Buku Lopatulika

Alendo anatha mphamvu yake osachidziwa iye; imvi zomwe zampakiza osachidziwa iye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Alendo anatha mphamvu yake osachidziwa iye; imvi zomwe zampakiza osachidziwa iye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Alendowo akuŵatha mphamvu, iwo osadziŵako. Akuyamba kumera imvi, iwo osadziŵako.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.

Onani mutuwo



Hoseya 7:9
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Hazaele mfumu ya Aramu anapsinja Israele masiku onse a Yehowahazi.


Pamenepo Pulo mfumu ya Asiriya anadza kudzamenyana ndi dziko, koma Menahemu anampatsa Pulo matalente a siliva chikwi chimodzi; kuti dzanja lake likhale naye kukhazikitsa ufumu m'dzanja lake.


Udzati, Anandimenya, osaphwetekedwa ine; anandikwapula, osamva ine; ndidzauka nthawi yanji? Ndidzafunafunanso vinyoyo.


Dziko lanu lili bwinja; mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; dziko lanu alendo alimkudya pamaso panu; ndipo lili labwinja monga lagubuduzidwa ndi alendo.


Inde, iwe sunamve; inde, sunadziwe; inde kuyambira kale khutu lako silinatsegudwe; pakuti ndinadziwa kuti iwe wachita mwachiwembu ndithu, ndipo unayesedwa wolakwa chibadwire.


Wolungama atayika, ndipo palibe munthu wosamalirapo; ndipo anthu achifundo atengedwa, palibe wolingalira kuti wolungama achotsedwa pa choipa chilinkudza.


Anthu anga aonongeka chifukwa cha kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala chilamulo cha Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.


Pakuti abzala mphepo, nadzakolola kamvulumvulu; alibe tirigu wosasenga; ngala siidzatulutsa ufa; chinkana iutulutsa, alendo adzaumeza.