Mudzawaika ngati ng'anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu. Yehova adzawatha m'kukwiya kwake, ndipo moto udzawanyeketsa.
Hoseya 7:6 - Buku Lopatulika Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng'anjo ya mkate, pokhala alikulalira; wootcha mkate wao agona usiku wonse, m'mawa iyaka ngati moto wa malawi. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng'anjo ya mkate, pokhala alikulalira; woocha mkate wao agona usiku wonse, m'mawa iyaka ngati moto wa malawi. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Mitima yao imatentha ngati uvuni ndi upo wao. Usiku wonse, ukali wao umanyeka, ndipo m'maŵa umayaka ngati moto. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto. |
Mudzawaika ngati ng'anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu. Yehova adzawatha m'kukwiya kwake, ndipo moto udzawanyeketsa.
Pakuti akapanda kuchita zoipa, samagona; ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwachokera.
Achigololo onsewo; akunga ng'anjo anaitenthetsa wootcha mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.
Onsewo atentha ngati ng'anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.
Tsoka iwo akulingirira chinyengo, ndi kukonza choipa pakama pao! Kutacha m'mawa achichita, popeza chikhozeka m'manja mwao.